Quantcast
Channel: Radio Maria Malawi
Viewing all articles
Browse latest Browse all 1875

Zigawenga za I.S Zanyonga Akhristu Makumi Awiri

$
0
0

Zigawenga za mgulu la Islamic State  I.S, zalengeza kuti zanyonga akhristu makumi awiri ndi mmodzi a mdziko la Egypt,omwe zidawagwira mdziko la Libya kumayambiliro a mwezi wa January chaka chino.

Lipoti lomwe gululo latulutsa pa makina a intaneti lati zigawengazo zachita chiwembucho, pobwezera imfa ya amayi ena achisilamu omwe adaphedwa mwankhanza mdziko la Egypt.

Padakali pano,dziko la Egypt silidatsimikize kuti akhristuwo ndi a mdzikolo, koma lati lili ndi mantha aakulu oti anthuwo atha kukhala a mdzikolo.


Viewing all articles
Browse latest Browse all 1875


<script src="https://jsc.adskeeper.com/r/s/rssing.com.1596347.js" async> </script>