Quantcast
Channel: Radio Maria Malawi
Viewing all articles
Browse latest Browse all 1875

Ophunzira a Chanco Ati Apitiriza Kunyanyala Maphunziro

$
0
0

Ophunzira pa sukulu ya ukachenjede ya Chancellor ati apitiliza kunyanyala maphunziro awo pokhapokha akulu-akulu a mu khonsolo yowona za maphunziro pa sukulu-yi (University Council) atabwera ndi maganizo otsitsa mtengo wa suluku fiziya ophunzira pa sukulu-yi.

M’tsogoleri wa ophunzira-wa Eunice James wanena izi pofotokozera Radio Maria Malawi amene amafuna kudziwa zambiri zokhudza nkhani ya kunyanyala kwa maphunziro komwe ophunzirawa akuchita pa sukuluyi.

Iye wati ophunzira pa sukulu-yi sasiya kuchita zionetsero zi kufikira akulu-akulu-wa, atamvera maganizo awo ndi kutsitsa mtengo watsopano wa ndalama za sukulu zolipilira maphunziro a pa sukulu-yi.


Viewing all articles
Browse latest Browse all 1875

Trending Articles


Mdima unadetsa dziko



<script src="https://jsc.adskeeper.com/r/s/rssing.com.1596347.js" async> </script>