Quantcast
Channel: Radio Maria Malawi
Viewing all articles
Browse latest Browse all 1875

Anthu Atatu Afa pa Ngozi ya pa Shoprite

$
0
0

Chiwerengero cha anthu omwe afa pa ngozi yomwe yachitikadzulopa Shoprite mu msewu wa Masauko-Chipembere mu mzinda wa Blantyreakuti chafika pa atatu.

Ngoziyi yachitika dzuro cha ku m’mawa, galimoto la mtundu wa lole lomwe anthu-wa omwe ati ndi mamembala akwaya ya mpingo wa CCAP anakwera, litaphonya msewu ndi kukagwera ku mbari ina ya msewu-wu.

Mamemala akwayawa akuti amachokera ku Luchenza m’boma la Thyolo kupita ku HHI kukachita nawo kwaya festival ya mpingo-wu.

Malinga ndi m’modzi mwa akuluakulu a Blantyre Synod ya mpingo wa CCAP, m’busa Moyenda Kanjerwa, anthu atatu omwe amwalira pa ngoziyi ndi a Christina Chitekwe omwe anafera pa malo angoziwo, a Anastanzia Mendulo komanso a Robert Ntopwa omwe amwalira akulandira thandizo la kuchipatala.


Viewing all articles
Browse latest Browse all 1875

Trending Articles


Mdima unadetsa dziko



<script src="https://jsc.adskeeper.com/r/s/rssing.com.1596347.js" async> </script>