Quantcast
Channel: Radio Maria Malawi
Viewing all articles
Browse latest Browse all 1875

EPISIKOPI WA DAYOSIZI YA BERGAMO AYENDERA RADIO MARIA MALAWI

$
0
0

Episikopi wa diyosizi ya Mangochi ya Mpingo wa Katolika Ambuye Allesandro Pagani ayamikira ubale umene ulipo pakati pa diyosiziyi ndi diyosizi  ya Bergamo m’dziko la Itary.

 

Ambuye Pagani alakhula izi  lolemba pamene Ambuye Francesco Beschi  a diyosizi ya Bergamo anayendera nyumba yofalutsira mawu ku Radio Maria Malawi m’boma la Mangochi.

Iwo ati amakhala okondwa nthawi zonse kamba koti dayosizi ya Bergamo imakhala ikuchita zinthu zosiyanasiyana zolimbikitsa ansembe ndi atumiki ena mu diyosiziyi yawo ya Mangochi maka omwe akutumikira m’chipani cha Mofolo woyera.

“Dayosizi ya Bergamo  ikuthandiza kwambiri ansembe athu kuno ku dayosizi yathu ya Mangochi,maka kwa iwo omwe akutumikira kuno ku Malawi kuchokera ku Italy”, atero Ambuye Pagani.

Ambuye Beschi anayenderanso nyumba yosindikiza  nkhani ya Montifort Media ku Balaka komwe athandiza ndi makina a makono osindikizira  mabuku a ndalama zoposa 50 miliyoni kwacha.

Ambuye Beschi akuyembekezekanso  kuyendera malo osiyasiyana mu diyosizi ya Mangochi.


Viewing all articles
Browse latest Browse all 1875

Trending Articles


Mdima unadetsa dziko