Quantcast
Channel: Radio Maria Malawi
Viewing all articles
Browse latest Browse all 1875

YCW Ikutolera Thandizo la Seminale Ya St. Peters

$
0
0

Bungwe la achinyamata mu mpingo wakatolika m’dziko muno la Young Christian Workers (YCW) lati likutolera thandizo pofuna kuthandiza seminale yaikulu ya St. Peters mu dayosizi ya Zomba yomwe padakali pano ikukumana ndi mavuto azachuma.

Wachiwiri kwa mtsogoleri wa bungweli mdziko muno, a Chrispin Ngunde anena izi polankhula ndi Radio Maria Malawi.

“Anatidziwitsa kuti seminaleyi ili ndi mavuto azachuma ndipo pa budget yawo ya chaka chino kuti amalize semester yomwe ikutha mu july muno ikusoweka 8 million kwacha ndipo tinavomera kuti titengapo gawo,” anatero a Ngunde.

A Ngunde ati ndi udindo wa achinyamata mu mpingo komanso akhristu eni ake kutengapo gawo pothandiza mpingo mu njira zosiyanasiyana pa nthawi yomwe ukukumana ndi mavuto.

“Mkhristu aliyense atha kutengapo gawo pothandiza mpingo kudzera munjira zosiyanasiyana zimene mpingowo watipempha. Sitingachite zonse ayi koma tithe kutengapo gawo lochepa lomwe tingakwanitse. Zimenezi zitha kuthandiza kuti mpingo wathu upite patsogolo ndiponso mpingo uthe kutifikira ife akhristu ndi kutithandiza monga tifunira kutinso tikathe kulandira mphotho yomwe mkhristu aliyense amayifuna yopita kumwamba,” anatero a Ngunde.


Viewing all articles
Browse latest Browse all 1875