Quantcast
Channel: Radio Maria Malawi
Viewing all articles
Browse latest Browse all 1875

Papa Fransisko Wayamikiridwa ndi Chipembezo cha Chisilamu

$
0
0

M’tsogoleri wa mpingo wakatolika pa dziko lonse Papa Francisco amuyamikira kamba kothilirapo ndemanga ponena kuti chipembedzo cha chisilamu si chofanana ndi magulu omwe amakhala akuchita za uchifwamba.

Mkulu wa chipembedzochi m’dziko la Iran, a Ayatolla Makarem Shirazi   walankhula izi kudzera mu kalata yomwe walemba pa tsamba lake la pa makina a Intaneti.

A Shirazi ati akugwilizana ndi mau omwe m’tsogoleri wa mpingo wakatolikayu analankhula kuti zauchifwamba zomwe zikuchitika m’maiko osiyanasiyana  sizichokera mu chipembedzo cha chisilamu.

Pamenepa a Shiraz anati apitiriza kumupemphelera Papa Francisco kuti apitirize kutumikira Mulungu.      


Viewing all articles
Browse latest Browse all 1875


<script src="https://jsc.adskeeper.com/r/s/rssing.com.1596347.js" async> </script>