Quantcast
Channel: Radio Maria Malawi
Viewing all articles
Browse latest Browse all 1875

Nthambi za Chitetezo Zidzudzula za Imfa ya Msilikali

$
0
0

Nthambi za chitetezo mdziko muno za Polisi ndi Army zadzudzula imfa ya msilikali wa Army yemwe anaphedwa ndi apolisi loweruka pa 22 November nthawi ya 11 koloko usiku mumzinda wa Zomba.

Akuluakulu ochokera munthambi ziwirizi adzudzula za imfayi pamsonkhano wa atolankhani omwe anachititsa lachinayi mu mzinda wa Lilongwe.

Akuluakuluwo adzudzula apolisi atatu omwe akukhudzidwa ndi imfa ya msilikaliyo,amene padakali pano ali mmanja mwa apolisi, ndipo alangiza asilikali munthambi ziwirizi kuti adzikhala ndi khalidwe pa ntchito yawo.

Polankhulapo nduna yowona za Chitetezo mdziko muno Paul Chibingu wati apolisi ntchito yawo ndi kupereka chitetezo kwa nzika za dziko lino ndipo kuti akamagwira ntchito yawo ayenera kutsata malamulo.

Iwo atsindika kuti akuluakulu a Army ndi Police mdziko muno akugwilira ntchito limodzi pofufuza za nkhaniyi kuti apeze chowona chenicheni.

Mkulu wa polisi a Paul Kanyama mogwirizana ndi mkulu wachiwiri  wa Army a Ignancio Maulana mdziko muno atsimikizira a Malawi kuti dziko lino lipitilira kukhala la bata ndi mtendere, ndipo ati mchitidwewu usagawanikitse dziko lino.

 

 


Viewing all articles
Browse latest Browse all 1875

Trending Articles


Mdima unadetsa dziko



<script src="https://jsc.adskeeper.com/r/s/rssing.com.1596347.js" async> </script>