Quantcast
Channel: Radio Maria Malawi
Viewing all articles
Browse latest Browse all 1875

Radio Maria Malawi Ithokoza Akhristu

$
0
0

Wachiwiri kwa mkulu woyang’anira  ma pulogalamu ku Radio Maria Malawi Bambo Charles Kaponya wayamikira akhristu kamba ka chidwi chawo potenga gawo  lothandiza wailesiyi.

Bambo Kaponya amalankhula izi pambuyo pa mwambo wa nsembe ya misa womwe unachitika lamulungu pa 30 November 2014 ku Ntcheu Parish mu dayosizi ya Dedza, womwe cholinga chake chinali chofuna kupeza thandizo lothandizira wayilesiyi.

Iwo analimbikitsa akhristu kuti apitilize kuthandiza wailesiyi kuti cholinga chake chipitilire kupita patsogolo.

Pamwambowu panapezeka ndalama zokwana 3 hundred and 35 thousand kwacha, matumba 7 achimanga ndi katundu wina osiyanasiyana.

Mwambo ngati womwewu unachitikanso ku St Pius Parish mu Arki Dayosizi ya Blantyre, polankhula  Bambo Mfumu wa Parishiyi Bambo Benito Masuwa anayamikira  abwenzi ndi anthu  onse kamba ka thandizo limene anapereka, ndipo pa mwambowu panapezeka ndalama zokwana 4 hundred and 19 thousand kwacha, komanso matumba awiri a chimanga.

 


Viewing all articles
Browse latest Browse all 1875

Trending Articles


Mdima unadetsa dziko



<script src="https://jsc.adskeeper.com/r/s/rssing.com.1596347.js" async> </script>