Quantcast
Channel: Radio Maria Malawi
Viewing all articles
Browse latest Browse all 1875

ANTHU 1 SAUZANDE AKUMATENGA MATENDA A EDZI PASABATA

$
0
0

 

Mlembi wamkulu mu ofesi yoona  za madyedwe ndi matenda a  Edzi Mai Edith  Mkawa  ati ndiwokhudzidwa ndi kufala kwa kachilombo ka matenda oyambitsa Edzi ka HIV ngakhale Boma likuyesetsa  kupeza njira zopewera kufala kwa matendawa.

M’dziko muno anthu 1 sauzande akumatenga matendawa pa sabata.

Mai Mkawa anena izi pa mwambo wokumbukira  matenda a Edzi omwe unakozedwa ndi nthambi yoona  za madyedwe komanso matenda a Edzi mu mzinda wa Lilongwe.

Iwo ati chiwerengero cha anthu otenga  matendawa chikukwera sabata iliyonse zomwe zikubwezera mbuyo  ntchito yolimbana ndi  kufala kwa matendawa.

“Ngakhale mauthenga onena zakuopsa kwa matendawa  akufalitsidwa, anthu sakusintha makhalidwe  awo komanso  ambiri  akusankha kukhala m’chimbulimbuli posakayezetsa magazi awo  kuti adziwe mmene mthupi mwawo muliri zomwe zikuchititsa kuti nthendayi idzifala chomwechi,”watero Mkawa.

Iwo ati  kuti boma  lingakwanitse kuthetsa kufala kwa kachilomboka  komanso imfa zomwe zimadza kamba  ka matendawa komanso  kusalana ngati anthufe  titachitapo kanthu.

“Kuyambira chaka cha 2011 mpaka 2015  mitu ya masiku okumbukira  matenda a Edzi  ikuunika 
njira zothetsera matendawa ndipo tiyeni a Malawi tiyesetse kuthandiza kuchepetsa  kufala kwa matendawa”, watero mlembiyu.

Iwo alangiza onse amene ali ndi matendawa kuti azidziteteza komanso kumwa mankhwala otalikitsa moyo.

“ Ndikulangiza onse amene anapezeka ndi kachilomboka kuti ayambe kulandira thandizo nsanga komanso kutsatira malangizo akuchipatala,” watero Mkawo.

Mkulu woona za ndondomeko ku bungwe la  National AIDS Commission (NAC) Mai Mirriam Mangochi   ati  anthu ambiri akumalephera  kukayezetsa kuti adziwe mmene thupi mwawo muliri kamba koopa kusalidwa komanso kukaima pamzere kuchipatala.

“Anthu akusankha kusadziwa mmene mthupi mwawo muliri kamba koopa kuti anthu awaona akaima pa mzere kuchipatala kuti alandire chithandizo.

Bungwe loona zaumoyo padziko lonse lapansi linaika pa 1 December kuti maiko,mabungwe komanso madera  adzikumbukira komanso kuganizira mmene angathetsere matenda a Edzi,

 


Viewing all articles
Browse latest Browse all 1875

Trending Articles


Mdima unadetsa dziko