Bungwe la Malawi Electoral Commission (MEC), lati nzika za m’dziko lino zikuyenera kuonetsa udindo wawo potenga mbali pazisankho zachaka cha mawa polembetsa m’nkaundula wa mavoti.
Wapampando wa bugweli mdziko muno a Justice Maxon Mbendera ndiye wanena izi mu mzinda wa Lilongwe pamene amalankhula ndi Radio Maria Malawi.
Justice Mbendera wati ntchito yolembetsa mkaundula wa zisankho ikuyembekezeka kuyamba pa 22 mwezi wa July chaka chino mpaka pa 4January chaka cha mawa.
“Aliyense akuyenera kulembetsanso kuti alandire chitupa chatsopano kamba koti zimphanso zakale zisidzagwiranso ntchito” watero Justice Mbendera.
Ntchitoyi igwiridwa m’magawo khumi kwa masiku 14 m’gawo
lililonse.