Quantcast
Viewing all articles
Browse latest Browse all 1875

Ambuye Msusa Asankhidwa Kukhala Apostolic Administrator wa Dayosizi ya Zomba

Mtsogoleri wa mpingo wa katolika padziko lonse Papa Francisco wasankha  Olemekezeka Ambuye Thomas Luke Msusa,omwe ndi arkepiskopi wa arkdayosizi ya Blantyre kukhala woyendetsa dayosizi ya Zomba ngati Apostolic Administrator,  mpaka pomwe episkopi watsopano  wa dayosiziyi adzasakhidwe.

Malinga ndi chikalata chomwe likulu la mpingowu latulutsa kudzera mwa kazembe wa mpingowu kuno ku Malawi ndi Zambia wolemekezeka Archbishop  Julio Murat ,Papa Francisco wasankha Ambuye Msusa kuti aziyang’aniranso dayosiziyi potsatira  imfa ya Monsignor Henry  Kaleso  omwe akhala akuyendetsa dayosiziyi.

Kudzera mchikalatachi, Olemekezeka Ambuye Murat apemphanso anthu kuti alumikizane  nawo popemphelera dayosiziyi komanso  Arc  Episkopi Thomas Luke Msusa  amene avomera udindo woyendetsa dayosizi ya Zomba poyembekezera episkopi  watsopano.


Viewing all articles
Browse latest Browse all 1875

Trending Articles


Mdima unadetsa dziko



<script src="https://jsc.adskeeper.com/r/s/rssing.com.1596347.js" async> </script>