Dziko la France lolemba lapereka ulemu wapadera kwa mzika zitatu za mdziko la America ndi ina yaku Britain chifukwa cholepheretsa munthu wina wamgulu la zaufwamba yemwe amafuna kupha anthu mu sitima yomwe imachokera mdziko la Germany paulendo opita ku France.
Mtsogoleri wa dzikolo Francois Hollande ndi yemwe wapereka ulemuwu kwa anthuwa.
Pulezidenti Hollande wati zomwe anthuwa achita zapereka chitsanzo chabwino pa zakufunika kolimba mtima pantchito yolimbana ndi mchitidwe wazauchifwamba omwe ukukulirakulira mmayiko osiyanasiyana.
Iye wati ndi zachidziwikire kuti pachiwembuchi anthu ambiri akanaphedwa koma kulimba mtima kwa anthuwa kwateteza zambiri.
Malipoti akusonyeza kuti panthawiyi musitimayo munali anthu mazana asanu.Pakadali pano akuluakulu a zachitetezo mdzikolo akufunsa mafunso munthu yemwe amafuna kuchita chiwembuchi yemwe ndi wa mdziko la Morocco.