Quantcast
Channel: Radio Maria Malawi
Viewing all articles
Browse latest Browse all 1875

Bungwe la UN Lawopseza Dziko la South Sudan

$
0
0

Bungwe la United Nations (UN) lawopseza kuti lichitapo kanthu ngati mtsogoleri wa dziko  la South Sudan a Salva Kiir  sasayina pangano la mtendere ndi magulu omwe akuwukira dzikolo.

Pa msonkhano wa atolankhani omwe nthambi ya zachitetezo  ku bungwelilinachititsa,   m`modzi mwa akuluakulu a bungweli a Stephen O`Brien ati padakali pano, zinthu sizili bwino ku South Sudanndipo mwazina anthu akumaotchedwa m`nyumba zawo.

Pulezidenti Kiir amayenera kuti asayine pangano la mtendere ndi cholinga choti  athetse kusamvana pakati pa boma lake ndi gulu  lowukira lomwe likutsogoleredwa ndi a Riek Machar omwe anasayinira kale panganoli.

Padakali pano anthu zikwizikwi aphedwa kale pankhondoyi ndipo ena opososa 2.2 million anathawa m`nyumba zawo.


Viewing all articles
Browse latest Browse all 1875

Trending Articles



<script src="https://jsc.adskeeper.com/r/s/rssing.com.1596347.js" async> </script>