Quantcast
Channel: Radio Maria Malawi
Viewing all articles
Browse latest Browse all 1875

Dziko la America Lithana ndi Zigawenga

$
0
0

M’tsogoleri wa dziko la America a Barack Obama wati dziko la America liyesetsa pothana ndi magulu a zigawenga omwe akulimbikitsa ziwembu m’mayiko  osiyanasiyana.

 

Iye walakhula izi pokhudzidwa ndi imfa ya anthu khumi ndi anayi omwe aphedwa pa chiwembu chomwe magulu ena a zauchifwamba achititira anthu okhala ku San Bernardino m’dzikomo.

 

Iye wati zomwe zachitikazi ndi zokhudza kwambiri choncho mkofunika kuti dziko lake litengepo mbali pa ntchito zowonetsetsa , kuti anthu a m’dzikomo akukhala mwa bata ndi mtendere.

 

Magulu a zigawenga omwe padakali pano ndi amene akusowetsa mtendere m’mayiko osiyanasiyana ndi monga la Islamic State IS lomwe linakachitanso chiwembu ndi kupha anthu oposera zana limodzi mdziko la France  la Boko Haram m’dziko la Nigeria ndinso la  Al Shabaab m’dziko Somalia.

M’tsogoleri wa dziko la America a Barack Obama wati dziko la America liyesetsa pothana ndi magulu a zigawenga omwe akulimbikitsa ziwembu m’mayiko  osiyanasiyana.

 

Iye walakhula izi pokhudzidwa ndi imfa ya anthu khumi ndi anayi omwe aphedwa pa chiwembu chomwe magulu ena a zauchifwamba achititira anthu okhala ku San Bernardino m’dzikomo.

 

Iye wati zomwe zachitikazi ndi zokhudza kwambiri choncho mkofunika kuti dziko lake litengepo mbali pa ntchito zowonetsetsa , kuti anthu a m’dzikomo akukhala mwa bata ndi mtendere.

 

Magulu a zigawenga omwe padakali pano ndi amene akusowetsa mtendere m’mayiko osiyanasiyana ndi monga la Islamic State IS lomwe linakachitanso chiwembu ndi kupha anthu oposera zana limodzi mdziko la France  la Boko Haram m’dziko la Nigeria ndinso la  Al Shabaab m’dziko Somalia.

M’tsogoleri wa dziko la America a Barack Obama wati dziko la America liyesetsa pothana ndi magulu a zigawenga omwe akulimbikitsa ziwembu m’mayiko  osiyanasiyana.

 

Iye walakhula izi pokhudzidwa ndi imfa ya anthu khumi ndi anayi omwe aphedwa pa chiwembu chomwe magulu ena a zauchifwamba achititira anthu okhala ku San Bernardino m’dzikomo.

 

Iye wati zomwe zachitikazi ndi zokhudza kwambiri choncho mkofunika kuti dziko lake litengepo mbali pa ntchito zowonetsetsa , kuti anthu a m’dzikomo akukhala mwa bata ndi mtendere.

 

Magulu a zigawenga omwe padakali pano ndi amene akusowetsa mtendere m’mayiko osiyanasiyana ndi monga la Islamic State IS lomwe linakachitanso chiwembu ndi kupha anthu oposera zana limodzi mdziko la France  la Boko Haram m’dziko la Nigeria ndinso la  Al Shabaab m’dziko Somalia.


Viewing all articles
Browse latest Browse all 1875

Trending Articles


Mdima unadetsa dziko



<script src="https://jsc.adskeeper.com/r/s/rssing.com.1596347.js" async> </script>