Ndege ina ya mdziko la Egypt yomwe inagwidwa ndi munthu wina ati yafika mdzikolo lachiwiri usiku munthuyo atadzipereka yekha kwa apolisi pa bwalo la ndege la Cyprus.
Ndegeyo nambala yake MS 181 inagwidwa ndi munthuyo yemwe anavala lamba wodziteteza ku chiwembu yemwe akuluakulu a ndegeyo atafufuza anazindikira kuti ndi lambayo anali wonamizira.
Padakali pano cholinga cha munthuyo pochita zomwe anachitazo sichinadziwike.
Malinga ndi malipoti a News 24 anthu 81 omwe anali mu ndegeyo sanavulazidwe.
Ndegeyo pomwe imagwidwa ati imachokera ku Alexandria kupita mu mzinda wa Cairo mdziko la Egypt.
Ndege ina ya mdziko la Egypt yomwe inagwidwa ndi munthu wina ati yafika mdzikolo lachiwiri usiku munthuyo atadzipereka yekha kwa apolisi pa bwalo la ndege la Cyprus.
Ndegeyo nambala yake MS 181 inagwidwa ndi munthuyo yemwe anavala lamba wodziteteza ku chiwembu yemwe akuluakulu a ndegeyo atafufuza anazindikira kuti ndi lambayo anali wonamizira.
Padakali pano cholinga cha munthuyo pochita zomwe anachitazo sichinadziwike.
Malinga ndi malipoti a News 24 anthu 81 omwe anali mu ndegeyo sanavulazidwe.
Ndegeyo pomwe imagwidwa ati imachokera ku Alexandria kupita mu mzinda wa Cairo mdziko la Egypt.