Bungwe lowona za mayeso mdziko muno la Malawi Examination Board (MANEB latulutsa zotsatira za mayeso a Malawi School Certificate of Education MSCE.
Malinga ndi wofalitsa nkhani ku unduna wa zamaphunziro, sayansi ndi Luso a Manfred Ndovi ophunzira 75 sauzande 2 hundred 96 ndi omwe achita bwino pa mayesowa ndipo mwa ophunzira 1 hundred ndi 36 sauzande 2 hundred 96 omwe analemba mayesowa.
Iwo ati zotsatira za mayeso a chaka chino zikusiyana ndi za chaka chatha kamba koti chaka chatha ophunzira 54 pa 100 aliwonse ndi omwe anachita bwino ndipo chaka chino ophunzira 55 pa ophunzira 100 aliwonse ndi omwe akhonza.
‘Tilimbikitse ophunzira onse omwe panopa ali form 4 kuti alimbikire maphunziro awo ndi cholinga choti chaka chamawa kankhonzedwe kadzakhale koposera chaka chino, anatero a Ndovi.’
Zotsatira za mayesowa zasonyezanso kuti anyamata ambiri ndi omwe ankhoza kusiyana ndi atsikana