Quantcast
Channel: Radio Maria Malawi
Viewing all articles
Browse latest Browse all 1875

Asilikali 17 Aphedwa Mdziko la Mali

$
0
0

Asilikali  pafupifupi 17 aphedwa ndipo ena makumi atatu 30 avulazidwa mu mzinda wa Nampala mdziko la Mali potsatira  chiwembu china  chomwe chachitika kumalo komwe asilikaliwa  amakhala.

Malinga ndi malipoti a wailesi ya BBC anthu omwe ananyamula zida zankhondo zoopsa anazungulira malowa ndi kuyatsa moto  mbali zina za malowo.

Magulu awiri  osiyana a zauchifwamba ati avomera kuti ndi omwe achita chiwembuchi ndipo ati achita izi ndi cholinga chobwezera chiwembu chomwe asilikaliwa anachita kwa anthu a mtundu wa Fulani.

Dziko la Mali ndi limodzi mwa maiko omwe muli magulu a zauchifwamba ambiri kuphatikizirapo gulu la zauchifwamba la Jihadist.


Viewing all articles
Browse latest Browse all 1875

Trending Articles


Mdima unadetsa dziko



<script src="https://jsc.adskeeper.com/r/s/rssing.com.1596347.js" async> </script>