Quantcast
Channel: Radio Maria Malawi
Viewing all articles
Browse latest Browse all 1875

ANTHU ASAFE NDI NJALA - VOICE OF THYOLO

$
0
0

Bungwe la Voice of Thyolo m`boma la Thyolo, ladzudzula boma, kaamba kolekelera kuti anthu omwe anathawa kudera la Mfumu yayikulu Ngonamo kwa Mfumu yayikulu Thomasi m`bomalo, adzimwalira ndi njala komanso kusowa zowayenereza pa moyo wawo watsiku ndi tsiku.

Wapampando wa bungweli a Harry Mikuwa, ndi yemwe  wanena izi potsatira imfa ya m`modzi mwa anthuwa a Gusto Paseli, omwe amwalira lolemba sabata yatha kumalo omwe anthuwa akusungidwa kwa Bvumbwe m`bomalo, kamba ka njala yomwe akuti yavuta kumalowa.Anthuwa anathawira kumalowo,gulu lina la m'mudzi mwa Wilson m’bomalo motsogozedwa ndi a Wilson Banda, litagwetsa nyumba ndikuwononga katundu wa fuko la a Ngonamo pomwe magulu awiriwa akhala akulimbirana ufumu wa a Ngonamo kwa zaka zingapo tsopano.


Viewing all articles
Browse latest Browse all 1875

Trending Articles


Mdima unadetsa dziko



<script src="https://jsc.adskeeper.com/r/s/rssing.com.1596347.js" async> </script>