Quantcast
Channel: Radio Maria Malawi
Viewing all articles
Browse latest Browse all 1875

Papa Apempha Akazembe Kuti Adzetse Mtendere

$
0
0

Mtsogoleri wa mpingo wakatolika pa dziko lonse Papa Francisco wapempha akazembe a m’maiko kuti awonenetsetse kuti akudzetsa mtendere popewa za mtopola mu ulamuliro wao.

Malinga ndi malipoti a wailesi ya Vatican Papa amalankhula izi ku likulu la mpingowu ndi akazembe a mmaiko a Burundi, Fiji, Mauritius, Moldova, Sweden, ndi Tunisia omwe amakapereka kalata zowayenereza kukhala ku likulu la mpingowu ngati akazembe.

Papa anauza akazembewa kuti agwilire ntchito limodzi pothetsa za mtopola  zomwe zikuchitika mmaiko osiyanasiyana.

Papa anankhula ndi akazembewa potsatira uthenga wa tsiku loganizira za mtendere lomwe ndi pa 1 January lomwe mutu wake ndi “Kuthetsa Zamtopola, Njira Ya Ndale Za Mtendere.”


Viewing all articles
Browse latest Browse all 1875


<script src="https://jsc.adskeeper.com/r/s/rssing.com.1596347.js" async> </script>