Quantcast
Channel: Radio Maria Malawi
Viewing all articles
Browse latest Browse all 1875

MOAM Yakhumudwa Ndi Anthu Okwera Minibus

$
0
0

Bungwe la eni minibus m’dziko muno laMinibus Owners Association of Malawi (MOAM) lati ndilokhumudwa  kuti anthu okwera ndi amene akuthandizira kuti ma minibus  m’dziko muno azinyamula anthu mopyola muyeso.

Bungweli  lanena izi posatila  ganizo laboma lofuna kuyamba kuyimitsa mtundu wa ma minibus za Vanneti komanso Bongo kuyenda pa msewu m’dziko muno ati ponena kuti galimotozi ndi zimene zikukolezera ngozi zambiri za pamsewu m’dziko muno.

“Ife tinawauza kuti solution sikuletsa ma vanneti kuyenda pansewu chifukwa galimoto zinanso ngati ma bus, ma lorry zimapezekanso zikunyamula anthu ochuluka kuposa mulingo wake. Inde vaneti ndiyaingono koma asaziletse kuyenda pansewu mwina dziko lingopanga malamulo ena okhuza zimenezi,” anatero a Kamange.

Iwo ati akanakonda boma likanakhazikitsa kuti woyendetsa amene apezeke atanyamula anthu ochuluka kupyola muyeso wake azimulanda chiphaso choyendetsera galimoto ndipo akapezeka atachita zimenezi kangapo azimuimitsa kuyenda pa nsewu kwa chaka.


Viewing all articles
Browse latest Browse all 1875

Trending Articles


Mdima unadetsa dziko



<script src="https://jsc.adskeeper.com/r/s/rssing.com.1596347.js" async> </script>