Quantcast
Channel: Radio Maria Malawi
Viewing all articles
Browse latest Browse all 1875

Dayosizi ya Mangochi Ilimbikitsa Achinyamata Kutenga Mbali mu Mpingo

$
0
0

Dayosizi ya mpingo wa katolika ya Mangochi yati iwonetsetsa kuti achinyamata akutenga nawo mbali pa zochitika zonse za mpingo.

Mlembi wa episkopi wa dayosiziyi bambo Steven Kamanga anena izi pa msonkhano wokhazikitsa bungwe latsopano loyang'anira achinyamata mu dayosiziyi lomwe akulitcha Youth Animation Team (YAT).

Iwo ati dayosiziyi yakonza dongosolo loti achinyamata azipezeka mu zochitika zilizonse za mpingo ndi cholinga choti agwilire ntchito limodzi kuti mapulani a dayosiziyi okweza achinyamata apite patsogolo.

Polankhulapo mkulu wa kuofesi yoona za achinyamata mu dayosiziyi, bambo Christopher Sichinga ati kubwera kwa gululi kuthandiza kuti ntchito zina za achinyamata zomwe zimavuta ziyambe kuyenda bwino.

Iwo ati ngakhale m’chaka cha 2016 akumana ndi zovuta zina koma chaka chino ayesetsa kuti akwaniritse zolinga zawo zonse zomwe akonza.


Viewing all articles
Browse latest Browse all 1875

Trending Articles


Mdima unadetsa dziko



<script src="https://jsc.adskeeper.com/r/s/rssing.com.1596347.js" async> </script>