Quantcast
Channel: Radio Maria Malawi
Viewing all articles
Browse latest Browse all 1875

Apempha Amayi Azitanganidwa Kukweza Dziko, Miyoyo Yawo

$
0
0

Amayi ochokera m’mipingo yosiyanasiyana m’dziko muno awapempha kuti azikonda kutanganidwa ndi zinthu zomwe zingathandize pa chitukuko cha miyoyo yawo ndi dziko lino.

Mayi Trizer Masauli omwe amatsogolera mwambo wa mapemphero a amayi ochokera m’mipingo yosiyanasiyana ya chikhristu, womwe wachitika pa 11 March 2017 m’boma la Mangochi ndi amene anena izi pakutha pa mwambo-wu.

Iwo ati nthawi yakwana yoti amayi achikhristu adzionetsa zitsanzo zabwino kuti mbiri yawo idzikhala yowala nthawi zonse.

Ku mwambo-wu kunafika amayi ochokera m’mpingo yoposera khumi ya chikhristu m’bomali.


Viewing all articles
Browse latest Browse all 1875

Trending Articles


Mdima unadetsa dziko



<script src="https://jsc.adskeeper.com/r/s/rssing.com.1596347.js" async> </script>