Quantcast
Channel: Radio Maria Malawi
Viewing all articles
Browse latest Browse all 1875

Chitukuko Chingapite Patsogolo Ngati Adindo ndi Mzika Akulumikizana

$
0
0

Kulumikizana pa nkhani za chitukuko cha m’madera pakati pa adindo komanso mzika ati ndi njira yokhayo yomwe ingapititse patsogolo chitukuko cha dziko lino.

Wachiwiri kwa mfumu ya mzinda wa Blantyre, a Wild Ndipo alankhula izi mu mzindawu ngati mlendo wolemekezeka pa msonkhano owunika momwe chitukuko cha maboma aang’ono chikuyendera pomwe mabungwe ndi anthu okhudzidwa pachitukuko amachita kawuniwuni pa momwe ntchito zachitukuko zikuyendera.

Iwo ati kusalumikizana pa nkhani zachitukuko cha m’madera sikoyenera, ichi ndi chifukwa chake nthumwi ku msonkhanowu zapeza kuti anthu ambiri akulephera kusamala chitukuko chomwe amalandira kamba ka vutoli.

Msonkhanowu omwe unakonzedwa ndi mabungwe a State of the Union, Eye for Development, Malawi Economic Justice Network {MEJN} komanso Citizen Alliance unasonkhanitsa makhansala, ma bwanamkubwa a mmaboma ena, akuluakulu a ku unduna wa maboma ang’onoang’ono komanso mabungwe.


Viewing all articles
Browse latest Browse all 1875

Trending Articles


Mdima unadetsa dziko



<script src="https://jsc.adskeeper.com/r/s/rssing.com.1596347.js" async> </script>