Quantcast
Channel: Radio Maria Malawi
Viewing all articles
Browse latest Browse all 1875

Mutharika Wati Atukula Mzinda wa Zomba

$
0
0

President wa dziko lino Professor Arthur Peter Mutharika wati boma lake likhazikitsa zitukuko zosiyanasiyana mu mzinda wa Zomba ndi cholinga choti mzindawu udzifanafana ndi mizinda ina ya mdziko muno.Mutharika amayankhula izi lachisanu atayendera misewu yatsopano yomwe  ikumangidwa mu mzindawu.

Iye wati mzinda wa Zomba uli ndi mbiri ya dziko lino motero ukuyenera kukhala ndi zinthu za makono.

“Ndikufunitsitsa kuti mzindawu upite patsogolo ndi program imeneyi ya misewu ndi maprogram ena. Tilinso ndi mapulani oti timange bwalo la masero a mpira wa miyendo la tsopano(stadium)paja pamene pali community ground. Tilinso ndi plan yoti timange Shopping Mall pafupi ndi Mulunguzi Centre,”anatero a Mutharika.

Iye wati boma lake likuchitanso ndondomeko yokonza magetsi onse mu misewu yonse ya mu mzindawu.

Mutharika anapezelaponso mwayi pa msonkhanowu kutsutsa zomwe zimamveka kuti pulezidentiyu pa msonkhano wake wachitukuko mboma la mulanje anati anthu azidya mbewa komanso zitete pa nthawi ino anthu mdziko muno akuvutika ndi mliri wa njala.

“Sabata yatha ndili ku Mulanje ndinanena kuti anthu ambiri amadalira chimanga chokha zomwe sizabwino. Chomcho ndinati anthu azidyanso mbatata, chinangwa komanso zicheche ena amati zilazi pachingerezi timati yams, sinnanene kuti zitete,” anatero Mutharika.

Boma la Mutharika latsimikizira anthu kuti likufuna kuthana ndi misewu yonse ya fumbi yomwe ili mmizinda yonse ya mdziko muno ndi kuyikamo phula.


Viewing all articles
Browse latest Browse all 1875

Trending Articles


Mdima unadetsa dziko



<script src="https://jsc.adskeeper.com/r/s/rssing.com.1596347.js" async> </script>