Mphepo ya mkuntho komanso ya mphamvu yaononga nyumba za anthu ndikusiya mabanja okwana 45,000 alibe malo okhala mu mzinda wa Queensland mdziko la Australia.
Malipoti a wailesi ya BBC ati nduna yaikulu ya mdzikolo a Malcolm Turnbull yalamula anthuwo kuti achoke kumalo wa omwe ati akuika miyoyo ya anthuwo pa chiopsezo chachikulu. M’chaka cha 2011, anthu oposa 25,000 a m’derali adapemphedwa kuti achoke ku malowo posatila mphepo ya ngati yomwe-yi imene inachitikanso m’chakacho.