Mtsogoleri wa mpingo wakatolika pa dziko lonse Papa Francisco wapempha akhristu a mpingowu kuti apempherere mtendere pa dziko lonse pansi.
Malingana ndi malipoti a wayilesi ya Vatican Papa Francisco wapeleka pempholi lamulungu pa bwalo la St Peter’s Square ku Vatican pomwe amalankhula kwa anthu omwe anasonkhana pa bwaloli.
Iye wati m’mapemphero a kolona a mwezi uno wa May akhristuwa akhale akupempherera mtendere pa dziko la pansi monga momwe Mayi Maria wa ku Fatima anapemphera.
Kumathero a sabata ino Papa Francisco akuyembekezeka kupita ku Fatima mdziko la Portugal komwe akakhale nawo pa mwambo okondwelera kuti patha zaka 100 chiwonekereni Amayi Maria ku malowo.