Radio Maria Malawi molumikizana wayilesi zina za Maria za pa dziko lonse lero zayamba ulendo wa masiku atatu wothamanga ndi amayi Maria mwa kathithi ndi cholinga chofuna kupeza thandizo la ndalama lothandizira wailesizi.
Wailesizi kuyambira lero kufikira lamulungu zikhala zikuwulutsa ma pologalamu apadera omemeza anthu kuti achitepo kanthu pofuna kukwaniritsa thandizoli.
Polankhula ndi mtolankhani wathu mkulu woona za ma pologalamu ku Radio Maria Malawi Bambo Joseph Kimu ati kuno ku Malawi ndalama yomwe ikuyembekezeka kutoleledwa ndi 28 miliyoni kwacha yomwe cholinga chake ndi kukonzeranso nyumba ya wailesiyi yowulutsira mau ku Mangochi, kukonzera ma transmitter onse omwe wailesiyi ili nawo, kumangira malo okhala popemphera pa goloto la amayi Maria komanso kugulira zida zowulutsira mau zoyenda nazo.