Makhansala a m’boma la Zomba atseka ma ofesi a mkulu woyang’anira mapulani ndi ntchito za zitukuko komanso ofesi ya mkulu woyang’anira ntchito zosiyanasiyana za m’bomalo kaamba kosakondwa ndi momwe akulu-akulu awiri-wa akugwilira ntchito zawo.
Wapampando wa Boma la Zomba Khansala Chikumbutso Likandawe wauza Radio Maria Malawi kuti aganiza zotseka maofesi-wa kaamba koti anthu awiri-wa akuwaganizira kuti akusakaza chuma cha khonsolo-yo.
Iwo ati zitukuko zambiri m’bomali sizikuoneka m’mene zikumathera ngakhale kuti ndalama zake zimakhala zitapelekedwa kale.
Koma poyankhulapo Bwana Mkubwa wa boma-li a Emmanuel Bambe wati sanayembekedzere kuona zomwe zachitikazi kaamba koti sanalandire dandaulo lililonse kuchokera kwa makhansala-wa.
M’malo mwake a Bambe ati akhala pansi ndi makhansla-wo kuti amve madandaulo awo. Pakadali pano a Willard Chirwa omwe ndi mkulu woyang’anira mapulani ndi chitukuko komanso a Hestings Mulambuzi omwe ndi mkulu woyang’anira ntchito za boma-li awatumiza ku tchuthi mokakamiza.