Quantcast
Channel: Radio Maria Malawi
Viewing all articles
Browse latest Browse all 1875

Maofesi A Mkulu Woona Za Chitukuko Ndi Ntchito Zina Atsekedwa.

$
0
0

Makhansala a m’boma la Zomba atseka ma ofesi a mkulu woyang’anira mapulani ndi ntchito za zitukuko komanso ofesi ya mkulu woyang’anira ntchito zosiyanasiyana za m’bomalo kaamba kosakondwa ndi momwe akulu-akulu awiri-wa akugwilira ntchito zawo.

 

Wapampando wa Boma la Zomba  Khansala Chikumbutso Likandawe wauza Radio Maria Malawi kuti aganiza zotseka maofesi-wa kaamba koti anthu awiri-wa akuwaganizira kuti akusakaza chuma cha khonsolo-yo.

Iwo ati zitukuko zambiri m’bomali sizikuoneka m’mene zikumathera ngakhale kuti ndalama zake zimakhala zitapelekedwa kale.

Koma poyankhulapo Bwana Mkubwa wa boma-li a Emmanuel  Bambe wati sanayembekedzere kuona zomwe zachitikazi kaamba koti sanalandire dandaulo lililonse kuchokera kwa makhansala-wa.

M’malo mwake a Bambe ati akhala pansi ndi makhansla-wo kuti amve madandaulo awo. Pakadali pano a Willard Chirwa omwe ndi mkulu woyang’anira mapulani ndi chitukuko komanso a Hestings Mulambuzi omwe ndi mkulu woyang’anira ntchito za boma-li awatumiza ku tchuthi mokakamiza.


Viewing all articles
Browse latest Browse all 1875


<script src="https://jsc.adskeeper.com/r/s/rssing.com.1596347.js" async> </script>