Quantcast
Channel: Radio Maria Malawi
Viewing all articles
Browse latest Browse all 1875

Amai a Mpingo Wakatolika Athandiza Seminare Ya St Peter’s.

$
0
0

Amai a bungwe la Catholic  Women Organization  (CWO)  m’dayosizi ya Zomba apereka katundu osiyanasiyana ku seminare yaikulu ya St Peter’s  m’bomalo.

 

Poyankhula ndi Radio Maria Malawi wapampando wa bungwe-li mu dayosizi-yi mai Elizabeth Meke wati bungwe lawo lipitiliza kuthandiza seminare-yi ndichlinga choti mpingo ukhale ndi ansembe ambiri.

 

Iwo ati akhristu ali ndi udindo wothandiza asemino-wa pa maphunziro ndinso umoyo wawo wa tsiku ndi tsiku kaamba koti nawonso ndi anthu ngati ife tomwe.

 

Ndipo Dikoni Charles Danken yemwe ndi mkulu woyang’anira a semino komanso madikoni pa seminare-yi wati ophunzira ku seminare-yi ndi osangalala kaamba koti anthu ambiri amawafunira zabwino pamene amawathandiza ndi zinthu zosiyanasiyana.


Viewing all articles
Browse latest Browse all 1875


<script src="https://jsc.adskeeper.com/r/s/rssing.com.1596347.js" async> </script>