Quantcast
Channel: Radio Maria Malawi
Viewing all articles
Browse latest Browse all 1875

Anankungwi Ndi Angaliba Awapempha Kuti Atulutse Msanga Zinamwali.

$
0
0

Mfumu Mpinganjira ya m’dera la mfumu yayikulu Mponda m’boma la Mangochi yapempha omwe alowetsa zinamwali m’bomali  kuti adzatulutse mwansana zinamwalizo.

 

Iyo yati kutulutsa nsanga zinamwali kudzapangitsa   kuti ana omwe ali ku zinamwaliwo adzakhale ndi nthawi yabwino yokonzekera kuyamba kwa telemu yawo yoyamba ya maphunziro a chaka cha 2017-2018.

Pamenepa mfumuyi yapemphanso mafumu kuti akuyenera kuonetsetsa kuti m’midzi mwawo , simukuchitika miyambo ndi zikhalidwe zina zosokoneza maphunziro a ana ndi cholinga choti ntchito za maphunziro zipitilire kuyenda bwino.

Polankhulanso m’phunzitsi wa mkulu pa sukulu ya pulayimale ya Changamire yomwe ikupezeka m’dera la mfumu yayikulu Mponda  a Jackson Gumbala wati kuchita Zinamwali sikolakwika , koma sizoyenera kuti zinamwalizo zizisokoneza maphunziro a ana.


Viewing all articles
Browse latest Browse all 1875


<script src="https://jsc.adskeeper.com/r/s/rssing.com.1596347.js" async> </script>