Quantcast
Channel: Radio Maria Malawi
Viewing all articles
Browse latest Browse all 1875

Bambo Wina Adzipha Ku Nkhotakota Pa Nkhani Za M’banja.

$
0
0

Bambo wina wa zaka 25 zakubadwa m’boma la Nkhotakota wadzipha podzimangilira atamvetsedwa kuti mkazi wake akuchita chibwenzi cha nseli ndi mwamuna wina.

Malingana ndi wachiwiri kwa ofalitsa nkhani za apolisi m’bomalo  Paul Malimwe,  malemu-yi Masauko Makiyi anadzipha pa 2 August kamba ka nkhani-yi.

Padakalipano apolisi ati apitiliza kufufuza mpaka atapeza zotsatira zeni zeni za  imfa ya malemuyi.

Malemuyi Masauko Makiyi  amachokera m’mudzi mwa Mvula m’dera la mfumu yayikulu Mphonde m’boma lomwelo la Nkhotakota. 


Viewing all articles
Browse latest Browse all 1875


<script src="https://jsc.adskeeper.com/r/s/rssing.com.1596347.js" async> </script>