Bambo wina wa zaka 34 zakubadwa wafa atagundidwa ndi galimoto pomwe amafuna kuwoloka nsewu pa m’sika wa Chezi m’boma la la Dowa.
Malingana ndi ofalitsa nkhani za a polisi m’bomalo Sergeant Richard Kaponda wati malemu-yi Jabesi Chipasula anagundidwa ndi min-bus yomwe imachokera ku Lilongwe kupita ku Salima pa 22 August 2017 pomwe amafuna kowoloka nsewu.
Malemu Jabesi Chipasula anali ochokera m’mudzi mwa Chadza mdera la mfumu yayikulu Kabudula mboma la Lilongwe.