Quantcast
Channel: Radio Maria Malawi
Viewing all articles
Browse latest Browse all 1875

Mwambo wolonga mfumu ya Angoni a kwa Njolomole uchitika mwezi wa September 2017.

$
0
0

Zokonzekera mwambo wolonga mfumu ya angoni a kwa njolomole akuti zikuyenda bwino.

Mwambo-wu udzachitika pa 21 September 2017 ku likulu la mfumuyi m’boma la Ntcheu.

Wapampando wa komiti yomwe ikuyendetsa za mwambo-wu Dr keneth wiyo ndi yemwe wanena izi pa 25 August 2017 pa msonkhano wa atolankhani mu m’dzinda wa Blantyre.

Iwo apempha angoni onse m’dziko muno kuti athandize komiti-yi ndi ndalama zoyendetsera mwambowu.

A Wilson Njolomole ndi omwe akukadzodzedwa kukhala inkosi njolomole ndipo izi zichitika kamba koti omwe anali mfumu ya angoni-wa anamwalira chaka chatha


Viewing all articles
Browse latest Browse all 1875


<script src="https://jsc.adskeeper.com/r/s/rssing.com.1596347.js" async> </script>