Quantcast
Channel: Radio Maria Malawi
Viewing all articles
Browse latest Browse all 1875

Zokonzekera Ulendo Wa Ku Malo Oyera Ku Rwanda Zikuyenda Bwino .

$
0
0

Komiti yomwe ikukonza ulendo wa ku malo oyera a Kibeho m’dziko la Rwanda  komwenso kuli mbiri ya   bungwe la Divine Mercy Apostolate yati padakalipano zonse zokonzera ulendowu zikuyenda bwino .

Wachiwiri kwa wapampando wa bungweli lomwenso ndi limene  lakonza ulendo-wu a Osward Bwemba  a ku Chigoneka Catholic Parish  mu Arch-Dayosizi ya Lilongwe  ati ulendo-wu ulipo pa pa 9 September 2017 ndipo onse amene apite ku malowa adzakabwelelako pa 16  mwezi womwe-wo.

Iwo ati bungwe lawo ndi lokondwa kuti chaka chino, akhristu a mbiri a mpingo wakatolika awonetsa chidwi chopita nawo ku malowa. 


Viewing all articles
Browse latest Browse all 1875


<script src="https://jsc.adskeeper.com/r/s/rssing.com.1596347.js" async> </script>