Quantcast
Channel: Radio Maria Malawi
Viewing all articles
Browse latest Browse all 1875

Papa Franciso Alimbikitsa Akhristu Kulimbika Popemphera Mapemphero A Kolona.

$
0
0

M’tsogoleri wa mpingo wakatolika pa dziko lonse papa Francisco walimbikitsa akhristu a mpingo wakatolika pa dziko lonse kuti asafooke koma kudzipereka pochita mapemphero a Kolona tsiku ndi tsiku.

Papa Francisco walankhula izi mu uthenga wake wokhudza mwezi uno wa October, umene wati ndi ofunika kwambiri mumbiri ya mpingo-wu, kamba koti ndi mwezi wolimbikitsa mapemphero a kolona omwe ndi othandiza kwambiri pa moyo wa chikhristu pakati pa akhristu-wa.

Pamenepa iye wati mwezi wa October ukuyenelanso kukhala mwezi wopemphelera onse omwe akudzipereka pogwira ntchito zosiyanasiyana zothandiza pa chitukuko cha mpingowu ndi mayiko awo. 


Viewing all articles
Browse latest Browse all 1875

Trending Articles


Mdima unadetsa dziko



<script src="https://jsc.adskeeper.com/r/s/rssing.com.1596347.js" async> </script>