Quantcast
Channel: Radio Maria Malawi
Viewing all articles
Browse latest Browse all 1875

Dr Chilima Alimbikitsa Za Mpingo Wodzidalira .

$
0
0

Akhristu a mpingo wakatolika mu dayosizi ya Mangochi awapempha kuti apitilize kudzipereka pothandiza mpingo-wu molowa manja .

Wachiwiri kwa m’tsogoleri wa dziko lino Dr Saulosi Chilima walankhula izi ngati mlendo wolemekezeka ku mwambo wa chaka chokondwelera nkhoswe ya dayosizi-yi. 

Pamenepa Dr Chilima ati akhristu a mpingo wakatolika mu dayosiziyi akuyenera kuti avale zilimbe pothandiza mpingo-wu molowa manja ndi modzipereka kamba koti tsopano mpingo-wu uli  m’manja mwawo chifukwa azungu omwe amathandiza mpingowu anabwelera kwawo. 

Mwambo wa chaka cha nkhoswe ya dayosizi ya Mangochi chinayamba ndi mwambo wa msembe ya misa yomwe anatsogolera ndi a episikopi a mpingo-wu mu dayosizi-yi  olemekezeka Ambuye Montfort Stima.

Mwazina akhristu-wa ku mwambo-wu athandizanso dayosizi yawo kudzera mu kugulitsa katundu wosiyanasiyana amene anabweletsa ndi cholinga chofuna kupeza ndalama zothandizira ntchito za dayosizi-yo.              


Viewing all articles
Browse latest Browse all 1875

Trending Articles


Mdima unadetsa dziko



<script src="https://jsc.adskeeper.com/r/s/rssing.com.1596347.js" async> </script>