Quantcast
Viewing all articles
Browse latest Browse all 1875

Apempha Boma Kulowererapo Pankhani Yakusowa Kwa Magetsi msukulu za Sekondare Zakumidzi Mdziko Muno.

Vuto la kusowa kwa magetsi m’sukulu za ku midzi akuti ndi limene likukoledzera mavuto a kusachita bwino pakati pa ophunzira m’sukuluzi pa maphunziro awo.

Wachiwiri kwa m’phunzitsi wa mkulu pa sukulu ya sekondale yoyendera ya Bvumbwe , m’boma la Thyolo , a Damiano Kondowe , ndi omwe anena izi polankhula ndi mtolankhani wathu. Iwo ati ana ambiri a msukuluzi amakhala ndi mzeru zokwanira , koma kuti amalephera kukonzekera bwino mayeso awo , kamba ka vuto la magetsi , panthawi yomwe afuna kuti awerenge nthawi ya usiku. Iwo apempha boma kuti pomwe likulimbikitsa zitukuko zosiyanasiyana  m’dziko muno lilimbikitsenso ntchito yopatutsa nthambo za magetsi kuti zifike msukuluzi , kuphatikizaponso ya Bvumbwe CDSS , yomwe ndi imodzi mwa sukulu zakale , koma kufikira pano ilibe magetsi. Iwo ati ngati boma lingachite izi ndiye kuti ana ambiri a msukuluzi azichita bwino pa maphunziro awo.


Viewing all articles
Browse latest Browse all 1875

Trending Articles


Mdima unadetsa dziko



<script src="https://jsc.adskeeper.com/r/s/rssing.com.1596347.js" async> </script>