Quantcast
Channel: Radio Maria Malawi
Viewing all articles
Browse latest Browse all 1875

Mnangagwa Alonjeza Ufulu wa Chibadwidwe ku Zimbabwe

$
0
0

Yemwe akuyembekezeka kukhala mtsogoleri wa dziko la Zimbabwe a Emmerson Mnangagwa wati akufuna kuti dzikolo likhale latsopano lomwe anthu ake akhale ndi ufulu wawo wachibadwidwe.

Malinga ndi malipoti  a wailesi ya BBC, Mnangagwa amalankhula izi ku likulu la dzikolo ku Harare atangofika kumene kuchoka mdziko la South Africa kutsatira kutula pansi udindo kwa a Mugabe omwe anali mtsogoleri wa dzikolo kwa zaka 37.

Mnangagwa walonjeza kukweza chuma cha dzikolo, kudzetsa mtendere mdzikomo komanso kupereka mwayi wa ntchito kwa anthu a mdzikolo pamene malipoti akusonyeza kuti anthu 90mwa 100 aliwonse sali pa ntchito mdzikolo.

Mkuluyu yemwe akuyembekezeka kulumbilitsidwa kukhala mtsogoleri wa dzikolo mawa lachisanu, wayamikira asilikali a dzikolo pothandizira kuchotsa a Mugabe pampando mwamtendere.

A Mugabe omwe padakali pano ali ndi zaka 93 ati atula pansi udindowo mwa kufuna kwawo pofuna kupereka mpata wosinthana ulamuliro wa dzikolo mwa bata ndi mtendere.


Viewing all articles
Browse latest Browse all 1875

Trending Articles



<script src="https://jsc.adskeeper.com/r/s/rssing.com.1596347.js" async> </script>