Wansembe yemwe anasowa masiku apitawa mdziko la Mexico akuti wapezeka atafa mdera lina lotchedwa Parras mdzikolo.
Malinga ndi malipoti a CNA wansembeyu Joaqui’n Hernandez yemwe amatumikira mu dayosizi ya Saltiloanasowa pa 3 mwezi uno ndipo wapezeka atafa patapita masiku 10 akumufufuza.
Malipoti ena akuti anthu awiri omwe sakudziwika analowa ku chipinda cha wansembuyu ndikumugwira komanso kumubera galimoto, makina a komputa ya mmanja kudzanso phone.
Pakadali pano anthu ena awiri omwe akuwaganizira kuti anachita nawo chiwembuchi agwidwa ndipo malipoti ena akusonyeza kuti galimoto lomwe linabedwali lapezeka pa mtunda wa makilomita pafupi 45 thousand omwe ndi ma miles 45