M’tsogoleri wa mpingo wakatolika pa dziko lonse papa Francisco waonetsa chitsanzo cha ubale wabwino pakati pa mpingo wakatolika ndi wa Anglican.
Papa wachita izi atakayendera akhristu a mpingo wa Anglican ku Parish ya mpingo-wu ya All Saints yomwe ikupezeka mu mzinda wa Rome m’dziko la Italy.
Malingana malipoti a wailesi ya kulikulu la mpingo wakatolika ku Vatican, Papa Francisco akuti wachita izi ngati njira imodzi yokondwelanso limodzi ndi mpingo-wu pomwe ukuchita chaka, cha zaka mazana awiri (200) chikhadzikitsileni tchalichi loyamba la mpingo-wu umene maziko ake ali m’dziko la England.