Quantcast
Channel: Radio Maria Malawi
Viewing all articles
Browse latest Browse all 1875

Akuluakulu a Bungwe la Utumiki wa Apapa Ayamikira Akhristu a Mpingo wakatolika Mdziko la Malawi

$
0
0

Akuluakulu a bungwe la utumiki wa apapa la Pontifical Missionary Societies PMS mmaiko a Britain ndi Ireland ayamikira akhristu a mpingo wakatolika mdziko muno kamba ka chidwi chawo pankhani zachipembedzo.

Mkulu wabungweli  mdziko muno bambo Vincent Mwakhwawa ndi womwe anena izi polankhula ndi Radio Maria Malawi pamene alendowa akuyendera zitukuko zomwe bungwe lawo lakhala likuthandiza mudayosizi ya Zomba.

Bambo Mwakhwawa ati alendowa achita chidwi powona zitukuko zosiyanasiyana zomwe akhristu achita modzidalira komanso mothandizidwa.

Paulendowu alendowa ayamikiranso  ana omwe akudzipereka kwathunthu mmabungwe a mumpingo.

Iwo apempha akatolika mdziko muno kuti atengere chitsanzo cha alendowa omwe akuti amapereka zochepa zomwe ali nazo pothandiza mpingo wa kuno ku Malawi.

Bungwe la utumiki wa apapa  linakhazikitsidwa mdziko muno ndi cholinga chofuna kulimbikitsa akhristu kuti azikhala odzipereka  potenga nawo mbali mu zochitika za mpingo.


Viewing all articles
Browse latest Browse all 1875


<script src="https://jsc.adskeeper.com/r/s/rssing.com.1596347.js" async> </script>