Quantcast
Channel: Radio Maria Malawi
Viewing all articles
Browse latest Browse all 1875

Dotolo Amwalira Atadwala Matenda a Ebola

$
0
0

Dotolo wina wa mpingo wakatolika amene wakhala akudzipeleka kwambiri pothandiza anthu odwala matenda a Ebola mdziko la Siera Lione akuti wamwalira atapezeka ndi matendawa.

Dotoloyo Martin Saliya yemwe anali ndi zaka 44 zakubadwa,akuti anali m’modzi mwa madotolo amene amagwira ntchito yawo modzipereka pothandiza anthu odwala matendawa mdzikolo, ndipo akuti wakhala akunenetsa kuti iye sangasiye kuthandiza anthu odwala  matenda a Ebola pofuna kuteteza moyo wake.

Kafukufuku wa bungwe la zaumoyo pa dziko lonse la World Health Organization wasonyeza kuti chibukileni matenda a Ebola chaka chino, anthu ogwira ntchito za umoyo omwe akhudzidwa ndi matendawa alipo 570 ndipo mwa anthuwa 354 amwalira.


Viewing all articles
Browse latest Browse all 1875

Trending Articles


Mdima unadetsa dziko