Quantcast
Channel: Radio Maria Malawi
Viewing all articles
Browse latest Browse all 1875

Apolisi Agwira Mzika Zina za Mdziko la DRC

$
0
0

Apolisi ku Chiponde m’boma la Mangochi, agwira mzika 34 za mdziko la Democratic Republic of Congo zomwe zimafuna kulowa mdziko la Mozambique kudzera mdziko muno mosavomerezeka.

Wofalitsa nkhani za apolisi m’bomalo Inspector Rodrick Maida,watsimikiza zankhaniyi.

Inspector Maida wati anthuwo, apezeka mderalo galimoto lina litawasiya pa malo ena mdera la mfumu yayikulu Jalasi m’bomalo.

Malinga ndi malipoti a apolisi,,mwa anthuwo asanu ndi awiri ndi akazi, ndipo atatu ndi ana.

Pakadali pano,anthuwo akuti awapereka mmanja mwa dipatimenti yowona za anthu olowa ndi otuluka mderalo kuti awathandize kubwerera kwawo ku Congo.


Viewing all articles
Browse latest Browse all 1875

Trending Articles


Mdima unadetsa dziko