Quantcast
Channel: Radio Maria Malawi
Viewing all articles
Browse latest Browse all 1875

MWAMUNA ADZIPHA PODZIMANGILIRA ATAKANGANA NDI MKAZI WAKE

$
0
0

Bozyolo  Chigwenembe wa zaka  22  zakubadwa wadzipha podzimangilira  pambuyo pokangana ndi  mkazi wake kwa mfumu yaikulu Dzoole m’boma la Dowa.

Mneneli wa apolisi ku Mponela  m'bomalo a Kondwani Kandiado ati  Chigwenembe adadzipha podzimangilira  kamba koti adasemphana mawu ndi mkaziyo, Bertha Nashe   wa zaka 19 zakubadwa.

Mkaziyo amadwaladwala zomwe zimamulepheretsa kugwira ntchito.

“A Chigwenembe adakwatira mkaziyo chaka chatha  koma wakhala akudwaladwala  zomwe zimachititsa kuti adzilephera kugwira ntchito za pakhomo, izi sizimasangalatsa malemuwo omwe anadzimangilira pogwilitsa ntchito nsalu”,anatero Kandiado.

Zotsatira za kuchipatala zawonetsanso kuti a Chigwenembe adamwalira kaamba kobanika.

Anthu anayi akuti ndi omwe afa podzimangilira pomwe asanu afa pomira m'madzi chaka chino chokha m'bomalo.


Viewing all articles
Browse latest Browse all 1875

Trending Articles


Mdima unadetsa dziko



<script src="https://jsc.adskeeper.com/r/s/rssing.com.1596347.js" async> </script>