Quantcast
Channel: Radio Maria Malawi
Viewing all articles
Browse latest Browse all 1875

Dziko la Burundi Lapempha Mzika zake Kupeleka Ndalama Zothandizira Chisankho

$
0
0

Dziko la Burundi  lapempha mzika za dzikolo  kuti zipereke ndalama zothandizira  pa  chisankho chomwe chikuyembekezeka kuchitika mdzikolo mwezi wa mawa.

 

Izi zadza pomwe bungwe la mgwirizano wa maiko aku ulaya la European Union (EU) layimika  thandizo la ndalama zoposa 2 million dollars  zomwe limayenera kupereka pothandizira kuyendetsa chisankhocho.

 

Anthu mdzikolo akhala akuchita  ziwonetsero posagwirizana ndi mfundo yoti mtsogoleri wadzikolo Pierre Nkuruzinza loti  apikisane nawo kachitatu paudindo wa pulezidenti.

 

Pulezidenti Nkuruzinza wati iye akuyenera kupikisana nawo pa chisankhocho  kamba koti mzaka zake zoyamba  kukhala pa udindowu anachita kusankhidwa ndi aphungu akunyumba yamalamulo ndipo chisankho chomwe  chidzachitike mdzikolo mwezi wa mawa kwa iye chidzakhala chachiwiri kuvoteredwa ndi anthu onse.


Viewing all articles
Browse latest Browse all 1875

Trending Articles


Mdima unadetsa dziko



<script src="https://jsc.adskeeper.com/r/s/rssing.com.1596347.js" async> </script>