Ma Volontiya wotumikila ku Mangochi Studiyo ya Radio Maria awalangiza kuti adzitsongoza Mulungu pamene akugwila tchito yotumikila kufalitsa uthenga wa Mulungu kudzela pa wailesiyi.
Bambo Elizeo Mtendere ananena izi Loweruka pa bindikilo womwe unachitikila ku Seminale yaying’ono ya St Paul ku Mangochi.
Bambo Mtendere analimbikitsa otumikila ku wailesiyi kuti adzidalila Mulungu pa zonse chifukwa chakuti,mwaiwo wonkha sangakwanitse.
“ Nyumba yomwe Ambuye samanga oyimanga ayimanga chabe”. Anatelo Bambo Mtendere.
Bambo Mtendere anayamikila utumikilawa pa ntchito yomwe amagwila yonthandiza kufalitsa unthenga wabwino Kudzera pa Wilesiyi.
Iwo anapitiliza kunena kuti kudzela pa Radio Maria miyoyo ya anthu ambiri ikusinthika ndipo nkoyenela kuti anthu amene akutumikila ku wailesiyi azionesa mankhalidwe abwino komanso azikonda kupemphera.
Mbindikirowu umakozedwa pakantha miyezi itatu iliyonse ndi cholinga chofuna kuzamitsa moyo wa uzimu wa anthu otumikira ku wailesiyi.
Ndipo Mutu wa Mbindikilowu unali woti “Kodi Anthu Amati Ndine Yani”,Kuchokera Mbuku Loyera pa Mateyu 16:13-19.