Quantcast
Channel: Radio Maria Malawi
Viewing all articles
Browse latest Browse all 1875

Boma la Malawi Ndilokonzeka Patchito Yotukula Mamphuziro a Atsikana.

$
0
0

President wa dziko lino   Professor Peter Mutharika wati boma lake ndi lodzipereka pantchito yotukura maphunziro aatsikana.

President Mutharika adayankhula zimenezi  pamsonkhano omwe unakonzedwa ndi bungwe la UN women  omwe  cholinga chake chinali kuunguza chidwi cha maiko amu Africa pankhani yothetsa maukwati a atsikana achichepere mkatikati mwa msonkhano wa bungwe la atsogoleri a m`maiko a Africa  wa Africa Union.

M`mawu ake mtsogoleri wadzikolinoyu anati boma la Malawi  ladzipereka kotheratu poonotsetsa kuti atsikana akukwatiwa  atafika zaka 18 ndipo kuti  dziko  la Malawi tsopano lili ndi lamulo  loti ana atsikana adzilowa m`banja atakwanitsa zaka 18 lomwe wati lakhala zaka 20 anthu asanalikambiranabe.

 Ndipo anawonjezela ponena kuti boma la Malawi limanganso ma hostel aatsikana ndicholinga chochepetsa mtunda omwe anawa amayenda akamapita kusukulu.

 Mmawu ake mkulu wa bungwe la UN Women Phunzile  Mlambo-Ngcuka anayamikira Purezideti Muntharika kamba kachidwi  chake  pomenyera ufulu wa atsikana pomwe malipoti akusonyeza kuti  atsikana  okwana 14 million  m`chigawo cha Sub Saharan  Africa  amachitiridwa nkhaza zosiyanasiyana .


Viewing all articles
Browse latest Browse all 1875

Trending Articles



<script src="https://jsc.adskeeper.com/r/s/rssing.com.1596347.js" async> </script>