Quantcast
Channel: Radio Maria Malawi
Viewing all articles
Browse latest Browse all 1875

MA EPISKOPI AKU AMERICA AYAMIKIRA AMECEA

$
0
0

Mpingo wa katolika mdziko la United States ndi bungwe la Catholic Relief Services[CRS] ayamikira bungwe la Association of Member Episcopal Conferences in Eastern Africa [AMECEA] kamba kodzipeleka pa ntchito zotukula miyoyo ya anthu okhala m’maiko a pansi pa bungweli.

Msonkhano wa atsogoleri a mpingo wa katolika a mmaiko a mchigawo cha AMECEA omwe ukuchitikira ku Bingu International Conference Center mumzinda wa Lilongwe unayamba pa 16 july ndipo uzatha pa 26 july 2014.

Poyankhula pomwe nthumwi za ku msonkhano wa AMECEA zimakonzekera zoyamba kuchita zokambilana zawo mumzinda wa Lilongwe, Pulezidenti wa bungwe la ma episkopi a m’dziko la United States Archbishop Joseph Tobin pamodzi ndi a Carlolyn Wool omwe ndi mkulu wa bungwe la CRS ati bungweli ladzipereka kwambiri pokweza ntchito za umoyo kuzanso maphunziro.

Bungwe la AMECEA linakhazikitsidwa mchaka cha1961 ndipo mamembala ake ndi maiko a Eritrea, Ethiopia, Kenya, Malawi, South Sudan, Sudan, Tanzania, Uganda and Zambia.

                                                                                       

 

 

 

 

 


Viewing all articles
Browse latest Browse all 1875


<script src="https://jsc.adskeeper.com/r/s/rssing.com.1596347.js" async> </script>