Quantcast
Channel: Radio Maria Malawi
Viewing all articles
Browse latest Browse all 1875

Ophuzira pa Sukulu ya Ukachenjede ya Lilongwe Technical Ayamba Kunyanyala Maphunzirowo

$
0
0

Ophunzira a pasukulu yosulira anthu maluso osiyanasiyana ya Lilongwe Technical ayamba kunyanyala maphunziro awo pokwiya ndi mavuto osiyanasiyana omwe akukumana nawo pa sukuluyo. Pulezidenti wa anthu omwe amaphunzira pasukuluyo Promise Daniel Chidothi wawuza Radio Maria Malawi mumzinda wa Lilongwe kuti ophunzira pa sukuluyi, akukumana ndi mavuto osiyanasiyana kuphatikizapo a zaumoyo. Chidothi wati ophunzira akudandaula kuti madzi mzimbudzi za pasukuluyi anasiya kutuluka zomwe zikuchitsa kuti azitenga madzi akafuna kukadzithandiza komanso kuti madzi akasamba mzipinda zosambira samachokamo. Iye anawonjezela ponena kuti akudandaulanso kuti patha chaka tsopano chipelekereni pempho kwa akuluakulu a pasukuluyo kuti ayambe kupereka maphunziro a makina a komputa kwa ophunzira a ntchito za manja, pofuna kuti nawo adziyendera limodzi ndi dziko pogwiritsa ntchito zipangizo zamakono koma mpaka pano palibe chomwe chikuchitika Radio Maria Malawi inalephera kumva zambiri kuchokera kwa akuluakulu a pasukuluyi kamba koti anali ndi zokambirana.


Viewing all articles
Browse latest Browse all 1875

Trending Articles


Mdima unadetsa dziko



<script src="https://jsc.adskeeper.com/r/s/rssing.com.1596347.js" async> </script>