Quantcast
Channel: Radio Maria Malawi
Viewing all articles
Browse latest Browse all 1875

Makampani Opanga Zakumwa Mdziko Muno Apereka Katundu Osiyanasiyana ku Chipatala Chachikulu cha Zomba

$
0
0

Makampani opanga zakumwa a Carsberg Malawi komanso Southern Bottlers apereka katundu osiyanasiyana othandizira pachipatala chachikulu cha Zomba.

 

Popereka katunduyu mneneri wa kampani ya Southern Bottlers Mayi Towera Munthali ati kampani yawo yapereka thandizoli powona  mavuto omwe chipatalachi chikukumana nawo pantchito yake yothandiza anthu.

 

Mayi Munthali ati malinga ndi kafukufuku wawo anapeza kuti ntchito zina pa chipatalacho  sizikuyenda bwino kamba  kakuchepa kwa zipangizo.

 

Polankhulapo mkulu wa chipatalacho Dr Mathias Joshua ati katunduyu wabwera  pa nthawi yake   kamba koti chipatalachi chikukumana ndi mavuto ambiri  monga kusowa kwa mankhwala komanso zipangizo zoyezera matenda osiyanasiyana.

 

Katundu yemwe waperekedwa pa chipatalachi ndi wokwana 77 miliyoni kwacha ndipo ma kampaniwa akugwira ntchitoyi mothandizidwa ndi mabungwe a City Hope International komanso Medi Care a mdziko la  Amerika mu zipatala za mdziko muno za  Ekwendeni m’boma la Mzimba, Queen Elizabeth mu mzinda wa Blantyre komanso Zomba Central.


Viewing all articles
Browse latest Browse all 1875

Trending Articles


Mdima unadetsa dziko